Anthu Anayi Amangidwa Kamba Koba Katundu
By Samson Kanyimbo………
Apolisi M’boma la Kasungu amanga anthu anayi powaganizira kuti anaba katundu okwana pafupafupi mamilioni.
Malingana ndi m’neneri wapolisi ya Kasungu, Joseph Kachikho , oganizilidwa-wa ndi Mphatso Ngozo Banda, Aubrey Lazimu, Jeremiah Phiri and Timothy Phiri ochokera m’boma la Kasungu omwe akhala akuzunguza m’madera osiyanasiyana m’bomali.
Kachikho wati apolisi akwanitsa kupulumutsa wailesi zakanema zitatu, Njinga ya moto, zipangizo zophikira ndi zina zambiri.
